Hosea 5

Chiweruzo cha Israeli

1“Ansembe inu, imvani izi!
Inu Aisraeli, tcherani khutu!
Inu nyumba yaufumu, mvetserani!
Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu:
Inu munali ngati msampha ku Mizipa,
munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
2Owukira azama mʼmoyo wakupha,
Ine ndidzawalanga onsewo.
3Ndimadziwa zonse za Efereimu;
Aisraeli ndi osabisika kwa Ine.
Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere;
Israeli wadziyipitsa.

4“Ntchito zawo siziwalola
kubwerera kwa Mulungu wawo.
Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere;
Iwo sadziwa Yehova.
5Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa;
Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo;
Yudanso anagwa nawo pamodzi.
6Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo
kukapereka nsembe kwa Yehova,
iwo sadzamupeza;
Iye wawachokera.
7Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova;
amabereka ana amʼchigololo
ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano
chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.

8“Womba lipenga mu Gibeya,
liza mbetete mu Rama.
Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni;
iwe Benjamini tsogolera.
9Efereimu adzasanduka bwinja
pa tsiku la chilango.
Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi
pakati pa mafuko a Israeli.
10Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu
amene amasuntha miyala ya mʼmalire.
Ndidzawakhutulira ukali wanga
ngati madzi a chigumula.
11Efereimu waponderezedwa,
akulangidwa chifukwa chotsatira
mafano.
12Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu,
ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.

13“Efereimu ataona nthenda yake,
ndi Yuda ataona zilonda zake,
pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya,
ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza.
Koma mfumuyo singathe kukuchizani,
singathe kuchiritsa mabala anu.
14Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu.
Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda.
Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo;
ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15Ndipo ndidzabwerera ku malo anga
mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo.
Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga;
mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”
Copyright information for NyaCCL